Chipani cha mlangizi wakale wa Renamo sichizachita masankho ku Mozambique
Chipani chatsopano cha mlangizi wakale wa Renamo Venancio Mondlane cha CAD, achikana kuti chidzapikisane nawo pa masankho omwe adzachitike pa 9 October chaka chino mdziko la Mozambique. Bright Sonjela akulongosola
Anthu ena ku Zambia adzudzula president Hichilema posintha nduna ya za umoyo
Mankhwala aboma la Zambia pa muyeso wa 65 million US dollars apezeka ku nkhokwe yosunga katundu yomwe ili mmanja mwa anthu wamba ,Mwa ichi, President Hakainde Hichilema wachotsa nduna ya za umoyo ,Sylvia Masebo, ndikuipereka ku unduna wa za nthaka. Anthu wamba ndi akuluakulu ena azipani zotsutsa…
Chiwelengelo cha anthu odzipha mdziko la Malawi chikuchulukila
Chiwelengelo cha anthu odzipha chikupitilira kukwela mdziko la Malawi Pamene anthu 256 anadzipha kuyambila m'mwezi wa January kufikila mwezi wa June Chaka chino chomwe ndi chokwela kuposela chaka chatha mnyengo ngati yomweyi, ndipo ambiri mwa anthu odzipha ndi abambo omwe akufika pa chiwelengelo …
Mtsogoleri wa Zambia wachotsa atsogoleri a bungwe lothana ndi katangale
Mtsogoleri wa dziko la Zambia Hakainde Hichilema wachotsa ntchito atsogoleri omwe anali mu bungwe lomwe limayang'anira chigao cha Anti-Corruption Commission chomwe chimalimbana ndi ziphupu komanso katangale mdzikolo . Mkulu wa bungwe la achinyamata la Youth Development Foundation, Muyeye Chinoya …
Mabungwe oyang’anila masankho ati masankho anayenda mwabata ku Rwanda
Mabungwe oyang’anira masankho omwe antenga malo mdziko la Rwanda, lero atulutsa lipoti la momwe masankho mdzikoli ayendetsedwera. Nzika za dziko la Rwanda zinaponya mavoti pa 15 July osankha mtsogoleri ndi aphungu a nyumba ya malamulo. Mtsogoleri wapakali pano Paul Kagame amapikisana ndi Frank Habe…
Anthu a ulumali ku Mozambique ati boma lipange njila zoti azivota pa masankho
Anthu a ulumali mdziko la Mozambique apempha boma kuti lipange njila zoti anthuwa azikhala ndi mwayi okaponya voti pamene anthu amalephela kukavota chifukwa cha mavuto osiyana siyana. Bright Sonjela akutambasula nkhaniyi
Akatswili a ndale ku Malawi ayankhulapo zakutuluka kwa a Kabambe mu DPP
A katswili a ndale mdziko la Malawi alankhulapo pa za kutuluka kwa Governor wakale wa bank ya reserve ya mdzikolo a Dalitso Kabambe atuluka mchipani chosutsa boma cha DPP pomwe ati achita izi chifukwa akufuna kupititsa patsogolo umoyo wawo wa ndale. George Mhango wabwela ndi nkhani yonse
Chipani cha UTM chatuluka mu Tonse Alliance mdziko la Malawi
Chipani cha United Transformation Movement -UTM cha mdziko la Malawi chalengeza kuti tsopano chatuluka mumgwirizano omwe chinapanga ndi chipani cha Malawi Congress Party -MCP otchedwa Tonse Alliance. izitu zanenedwa pamsonkhano wa atolankhani lero mumzinda wa Lilongwe. Mtolankhani mzathu Kondwan…
President wa dziko la Botswana Mokgweetsi Masisi akucheza ku Mozambique
President wa dziko la Botswana Mokgweetsi Masisi akucheza mdziko la Mozambique kufikila lachisanu sabata ino komwe akambilane zolimbitsa ubale pakati pa mayikowa. Bright Sonjela akufotokoza
Banki ya Zambia ili ndi cholinga choletsa kugwilitsa ntchito ndalama za kunja
Banki yaikulu ya mdziko la Zambia ya Bank of Zambia ikukonza chiganizo chakuyimitsa kugwiritsa ntchito ndalama zaku maiko akunja mu ntchito zamalonda zomwe zimachitika mkati mwa dzikolo. Bankiyi ili ndi maganizo akuti chiletso chimenechi chidzalimbitsa mphamvu za ndalama ya kwacha komanso maziko a…