

Msonkhano wa zi ntchito za njanji wa Africa Rail wamalizika
Msonkhano wa zi ntchito za njanji wa Africa Rail wamalizika lero. Msonkhanowu, omwe unali wa masiku awiri, umachitikira pa malo otchedwa Sandton Convention Centre mzinda wa Johannesburg mchigawo cha Gauteng mdziko la South Africa ndipo cholinga chake chinali kufuna kukambirana mwa njira zina zomwe …

Mabungwe ena ku Zambia ati a Hichilema asapange kampeni ndi katundu wa boma
Bungwe la Transparency International Zambia , lomwe limalimbikitsa ulamuliro wabwino ndi kulimbana ndi ziphuphu m'dziko la Zambia, lapempha Purezidenti Hakainde Hichilema kusiya kugwiritsa ntchito katundu wa boma pochita kampeni ya masankho. Mkulu wa bungweli, Maurice Nyambe, ndi amene wapereka pem…

Chionetselo cha za malonda cha Internationational Trade Fair chatha ku Zambia
Chionetselo cha za molonda cha International Trade Fair chafika lero kumapeto mdziko la Zambia komwe mayiko 23 anatenga nawo mbali pamodzi ndi nthumwi zoposa 1000. Ziyenela Zimba wadza ndi zambiri.

Aphungu atsegulira nyumba ya malamulo ku Malawi
A phungu a nyumba ya malamulo mdziko la Malawi, ayamba zokambirana zawo lero za chi number 52. Uwutu ndi mkumano wa chitatu chisinthireni boma kupita m’manja mwa President Arthur Peter Mutharika. Kondwani Nyamasauka ali ndi nkhani yonse

Mozambique apeleka ntchito kwa mzika zomwe zathawa ku South Africa
Boma la Mozambique lati anthu amene anathamangitsidwa ku South Africa awayika mu ma projekiti a ntchito zosiyana siyana kuti akhale ndi mwayi wa ntchito. Bright Sonjela akufotokoza zambiri

Malawi akukondwelera zaka 62 za ufulu odzilamulira
Anthu a mdziko la Malawi ati dzikolo silikutukuka mu zinthu zambiri ngakhale likukondwelera kuti lakwanitsa zaka 62 chikhalireni pa ufulu odzilamulira kuyambila mchaka cha 1964. Jayne Chilamampunga wamva maganizo katswili olankhula pa nkhani zosiyana siyana mdzikolo a Imran Saidi

Bungwe la ECZ ku Zambia lakana za kutsindika mapepala ena ovotela mwa chinsisi
Bungwe lowona za masankho mdziko la Zambia la ECZ lakana kuti likutsindika ma pepala owonjezela ovotela mwa chinsisi. Ziyenela Zimba akufotokoza

Loya wa Kizza Besigye ku Uganda azaonekela ku khothi pa 9 Julaye
Khothi la Machindye ku Kampala mdziko la Uganda, layimitsa kumva mlandu wa loya komanso mtsogoleri wa chipani cha People's Front for Freedom, Erias Lukwago, womwe ukumuneneza mlandu wofuna kulanda.Khothilo lati Lukwago sanathe kubwera kukhoti chifukwa akulandira chithandizo chapadera kuchipatala at…

Anthu a mu bizinesi ang’ono ku Zambia akupempha boma kuti liwapatse ngongole
Anthu ochita za malonda ang’ono ang’ono mdziko la Zambia apempha boma kuti liwathandize ndi ngongole ya ndalama zochitila ma business awo . Ziyenela Zimba walankhula ndi m’modzi mwa anthu amene amachita malonda a mtunduwu bambo Adrian Banda.

Mzika 51 za ku Mozambique zawotcheledwa nyumba ku South Africa
Anthu okwana 51 a mdziko la Mozambique amene akukhala ku South Africa akusowa pokhala pamene nyumba zawo pomodzi ndi katundu zaotchedwa m’dela la Mamelodi mu mzinda wa Pretoria. Bright Sonjela akufotokoza nkhani yonse