



Mabungwe ena ku Malawi adzudzula zomwe Alexious Kamangila akulankhula
Mabungwe omenyela ma ufulu a anthu mdziko la Malawi a MABLEM ndi HRCC adzudzula mchitidwe ogwilitsa ntchito masamba amchezo molakwikika pamene loya wina Alexious Kamangila akutchula akulu akulu ena kuti akuchita za katangale . Jayne Chilimampunga wabwela ndi nkhani yonse

A katswili andale ena ku Malawi ati a Chakwera sanalankhule bwino pa maliro
Zomwe anayankhula mtsogoleri wakale wa dziko la Malawi Dr Lazarus Chakwera kuti anthu asamutengere ku mtoso ndi munthu okonda mtendere zautsa zoyankhula zosiyana pakati pa Malawi. Mtolankhani mzathu mdziko la Malawi Kondwani Nyamasauka ali ndi nkhani yonse.

Mtsogoleri wa South Sudan Salva Kiir wachotsa sipikala wa nyumba ya Malamulo
Purezidenti wa dziko la South Sudan, Salva Kiir, wachotsa ntchito Spikala wa Nyumba ya Malamulo komanso wachiwiri wake. Muchidziwitso chomwe chalengezedwa m’Nyumba ya Malamulo Lachiwiri ndi Tulio Odongi Ayahu, yemwe ndi mkulu wa chipani cholamula cha SPLM ,chati amene achotsedwa ndi Jemma Nunu Kumb…

Mchitidwe wa anthu otengela lamulo m’manja wakula ku Zambia
Boma la dziko la Zambia liri ndi nkhawa ndi mchitidwe wa anthu otengela lamulo m’manja mwawo pamene munthu wapalamula ndipo polisi yati izathana ndi aliyense ochita zimenezi. Ziyenela Zimba wabwela ndi nkhani yonse

Mafuta agalimoto akwera ku Malawi ndi 35%
Mafuta a galimoto ndi ndege akwera kwambiri mdziko la Malawi zomwe zikupereka chiopsezo kuti mwina zinthu zofunikila pamoyo wa anthu zikwera mtengo. Mafuta a petrol akwera ndi 34 % kufika pa K6,672 kuchoka pa K4,935 ndipo Dizilo wakwela ndi 35% kufika pa mtengo wa K6,687 kuchoka pa K4,945 . Mt…

Anthu 300 amangidwa ku Zambia Kamba kopha mayi wina pomuganizila kuti ndi mfiti
Anthu pafupifupi 300 amene akukhudzidwa ndi kuphedwa mwa nkhanza kwa mai wa ntchito za malonda, Hellen Kamutumbe , amangidwa ndi A polisi mu boma la Kalumbila ku chigao cha North-western Province cha dziko la Zambia. Maiyu anavulidwa ndi kugendedwa miyala ndi anthu okwiya Lachisanu lathali pamene …

Apolisi ku Kenya amanga nduna yakale chifukwa chonamizila kubedwa
Raphael Tuju, yemwe ndi Nduna yakale yoona za ubale pakati pa dziko la Kenya ndi mayiko ena , amupeza ndipo amumanga kamba konamilizira kuti wasowa komanso kuti anabedwa.Mkulu wotsogolera kafukufuku ku polisi ya Nairobi a Mohamed Amin, anena pa msonkhano wa atolankhani kuti a Tuju anali mkati mwa …

Nyumba ya malamulo ku Malawi yakhazikitsa komiti yofufuza imfa ya a Chilima
Sipikala wa nyumba ya malamulo ya mdziko la Malawi Sameer Suleman wakhazikitsa committee yatsopano yapadela yomwe ichite yakafuku fuku wa ngozi yomwe inapha wachiwiri kwa president Dr Saulos Chilima ndi anthu ena asanu ndi atatu ndipo ku committee imeneyi mukhala aphungu oyima pa okha ndi aphun…

Mtsogoleri wachipani chotsutsa cha NUP ku Uganda Bobi Wine watuluka mdzikolo
Mtsogoleri wachipani chotsutsa boma cha National Unity Platform NUP ku Uganda a Robert Chagulanyi Sentamu omwe amadziwikanso kuti Bobi Wine atuluka m'dziko la Uganda. Zifukwa zeni zeni zomwe iwo atulukira mdzikolo sizikudziwika koma a Bobi Wine akhala akunena kuti moyo wawo unali pa chiopsyezo ndi…

Achinyamata ku Zambia ati achinyamata apatsidwe mwayi otukula miyoyo yawo
Zigao zonse khumi za dziko la Zambia lero zachita chisangalalo cha achinyamata cha Youth Day ndipo chapmutu cha chaka chino chili motere: Dzukani ndi Kuuluka . Koma chisangalalo chachikulu cha dziko lonse chayendetsedwa ndi President Hakainde Hichilema mu boma la Solwezi ku chigao cha North-wester…