Mai Regina Joyce Matsinhe yemwe ndi mkulu oona zintchito za kayendetsedwe ka masankho mu bungwe la Electoral Administration mdzikoli ,ati bungweli lakhazikitsa malo oponyera ma voti okwana 26 327, kuphatikiza malo okwana 600 m’maiko ena. Anthu okwana 17 million alembetsa kuti atenga nawo gawo pa masankhowa, ndipo chiwerengerochi ndi chokwera ndi 29 percenti kuyerekeza ndi mchaka cha 2019. Thamo Kapisa ali ndi nkhaniyi