



Mada Phiri kucheza ndikatswili oyimba wa mdziko la DRC Feed Paul RP amene amadziwika
Ndidzina lokuti Feed RP, pamene akunene za mmene anayambila luso lake loyimba muchaka cha 2010 Komaso pokhala ku misasa yosiyana mdziko la Malawi kumene kunachititsa kuti adziwe kuyankhula Chichewa.

Oyimba wa manganje wa ku Mozambique Ricabana wati amanyadila kuyimba za chimidzi
Oyimba wa manganje wa ku Mozambique Ricabana, wati amanyadila kuyimba za chimidzi ndipo apitilira kuyimba nyimbo za chikhalidwe ngakhale akukumana ndi mavuto osiysa siyana. Stella Longwe walankhula ndi oyimbayu pa programu ya Malonje

Gulu la akatswili opanga ndikusoka zovala zosiyana siyana la PSV Luxury, ladziko la Malawi koma amakhala mdziko la South Africa, kucheza ndi Mada Phiri ndikutiuza mmene anayambila ntchito yawo

MONEY MIKE INTERVIEW
Kucheza ndi katswili wazoimba imba wadziko la South Africa Money Mike, pamene watiuza kuti wapanga ngwilizano ndi nyumba yaikulu yojambula nyimbo yaku America ya Sonny komaso ya Rico Nation, ndi kutulutsa nyimbo yake yotchedwa Alhamdulila.

Oyimba wa Ku Malawi L Nowa wati oyimba aziwona patsogolo
Oyimba wa Ku Malawi amene amakhala mdziko la South Africa L Nowa, wati oyimba asamamvele zokamba kamba koma azipita chitsogolo kuti azipitilira ndi luso lawo loyimba. Stella Longwe anacheza ndi oyimbayu pa program ya Malonje

Kucheza ndi Starval oyimba wa ku Malawi
Katswili oyimba wa ku Malawi amene akuyimba mdziko la South Africa Starval Stevens, wati chidwi choyimba ndi chomwe chimapangitsa oyimba kuti apitilire kuyimba ngakhale akukumana ndi zovuta zambiri. Stella Longwe wacheza ndi katswiliyu.

Kucheza ndi katswili wazoimba imba mdziko la Malawi Waxy Kay
Kucheza ndi katswili wazoimba imba mdziko la Malawi Waxy Kay, pamene anatiuza za ulendo wake wa kudziko la South Africa, komaso kuimba ku birthday ya mzake.

Pali kugawikana pakati pa boma la Zambia ndi Tonse Alliance za maliro a aLungu
Pali kugawikana maganizo pakati pa boma la zambia ndi mgwilizano wa zipani zosutsa boma wa Tonse Alliance za ku malo oli-li-ra maliro a prezidenti wakale wa Zambia Edgar Chagwa Lungu pamene boma la dzikolo layimitsa kuti thupi la malemu Lungu linyamuke kuchoka mdziko la South Africa kupita ku Zambi…

Mwambo okumbukila malemu Saulosi Chilima wachitika ku Malawi
President wa dziko la Malawi Dr Lazarus Chakwera,anatsogolera a Malawi pa mwambo okumbukila malemu Saulos Chilima yemwe anali wachiwiri wawo ndipo mwambowu unachitikira m’boma la Mzimba pamene akubanja nawo anali ndi mwambo ngati omwewu ku kumudzi kwa Chilima m’boma la ntcheu. Mtolankhani mzathu m…

Ripoti lomaliza la ngozi ya ndege yomwe inapha a Chilima ku Malawi latuluka
Ripoti lomaliza la ngozi ya ndege yomwe inapha wachiwiri kwa president Dr Saulos Chilima ndi anthu ena asanu ndi atatu 8 pa 10 June chaka chatha, latulutsidwa ndi Nthambi yochita kafuku fuku wa ngozi za ndege mdziko la Germany ya Germany Federal Bureau of Air craft accident investigations ya BFU. …