Khothi ku South Africa lati president wakale Zuma asazayime pa masankhoKatswili owona zochitika mu Africa Comrade Dr Griffin Maruwasa, wati chipani chotsutsa boma cha mdziko la South Africa cha Umkhonto we Sizwe (MK), chili pa chiopsezo potsatila chigamulo cha khothi la Constitutional la mdzikolo, chokuti mtsogoleri wa chipanichi Jacob Zuma, amenenso ndi president wakale wa dziko la South Africa, asadzayime nawo pa masankho a president ndi aphungu anyumba ya malamulo omwe adzachitike pa 29 May chaka chino, chifukwa chokuti analandila chilango chophika ndende kwa miyezi 15 mchaka cha 2021.
Stella Longwe walankhula ndi katswiliyu .