Zipani zina zotsutsa boma ku Zambia sizikufuna kuwonjezela aphungu 70Zipani zingapo zotsutsa boma mdziko la Zambia kuphatikizapo chipani cha Forum for Democracy and Development, FDD, ndi mabungwe ena wodziyimira pa okha, akana kutengako mbali ku zokambilana zakuchulukitsa chiwerengero cha aphungu ndi 70. Bungwe lomwe limayendetsa zisankho mdzikolo la Electoral Commission of Zambia, ECZ, layambitsa ntchito yakufunsila maganizo ya mafumu, atsogoleri aza ndale, amipingo ndi ena Lolemba pa 16 February 2026. Daniel Elisha Banda akusimba.