Africa yakumbukilidwa pomwe ikuona mavuto osiyana siyanaMaiko a mu Africa,akumbukira tsiku lotchedwa Africa Day. Tsikuli linakhazikitsidwa ndi cholinga chofuna kulimbikitsa nzika za kufunika kwa maiko kukhala pa ma ufulu odzilamulira paokha, komanso kuyanjana. Tsikuli, likukumbukiridwa pomwe anthu m'maiko monga a South Sudan, Sudan, DRC, ndi okhala ku Cabo Delgado kumpoto kwa Mozambique, akupitilira kukumana ndi mabvuto chifukwa cha nkhondo ndi mikangano. Bambo Melton Luhanga m'modzi mwa nthumwi zoimilira bungwe loteteza ma ufulu a anthu othawa kwawo ku m'mwera kwa Africa la SAMIN, alankhula ndi wailesi ino ya Channel Africa. Thamo Kapisa ali ndi ripoti ili.