Mabungwe ena ku Zambia ati a Hichilema asapange kampeni ndi katundu wa bomaBungwe la Transparency International Zambia , lomwe limalimbikitsa ulamuliro wabwino ndi kulimbana ndi ziphuphu m'dziko la Zambia, lapempha Purezidenti Hakainde Hichilema kusiya kugwiritsa ntchito katundu wa boma pochita kampeni ya masankho. Mkulu wa bungweli, Maurice Nyambe, ndi amene wapereka pempholi pamene dziko la Zambia likuyembekezera masankho apatatu pa 13 August 2026. Daniel Elisha Banda ali ndi nkhani yonse