Loya wa Kizza Besigye ku Uganda azaonekela ku khothi pa 9 JulayeKhothi la Machindye ku Kampala mdziko la Uganda, layimitsa kumva mlandu wa loya komanso mtsogoleri wa chipani cha People's Front for Freedom, Erias Lukwago, womwe ukumuneneza mlandu wofuna kulanda.
Khothilo lati Lukwago sanathe kubwera kukhoti chifukwa akulandira chithandizo chapadera kuchipatala atadwala ali m'ndende.
Mlanduwu uyambiranso pa 9 Julayi, pamene khothi lidzalandire lipoti la thanzi lake komanso momwe kafukufuku wa boma ukuyendera. Alfred Dzaoneni ali ndi zambiri